Langwan Piksy – Wako Wako lyrics

VERSE 1
Uthenga wa masankha kwa Namazanje
Panopa tiri official si za masanje
Lero sitisamala za wansanje
Tivine ingoma
Mkhetekete ndi manganje
CHORUS
Tinafunitsitsa banja titamanga
Koma tinadziwa kufika si ku thamanga
Ona lero ndine wako wako
Ndine wako wako
Ona lero ndine wako wako
Ndine wako wako
VERSE 2
Ulendo wathu tangoyamba komano tikafika
Kaya mitunda tikwera ndi 0p titsika
Tilowa pena mmatope pena tiponda minga
Koma chimodzi ndikhulupira Yehova ndi Linga
Tiyenda mu dzuwa
Mvula
Limodzi tikula
Ukumva?
Namazanje
CHORUS
Tinafunitsitsa banja titamanga
Koma tinadziwa kufika si ku thamanga
Ona lero ndine wako wako
Ndine wako wako
Ona lero ndine wako wako
Ndine wako wako
VERSE 3
Poti ndasankha iweyo kuti ndikupatse wanga mtima
Poti ndasankha iweyo kaya mokhwepa ndi mothina
Honey ndasankha iweyo kaya kuwala kaya mdima
Ine ndasankha iweyo kuti tikhale mpaka muyaya
Ndasankha iwe
Poti ndasankha iwe
Poti ndasankha iweyo honey
Ndasankha iweyo Namazanje
CHORUS
Tinafunitsitsa banja titamanga
Koma tinadziwa kufika si ku thamanga
Ona lero ndine wako wako
Ndine wako wako
Ona lero ndine wako wako
Ndine wako wako

Leave a Comment

error: Content is protected !!